가사
Intro
Thindimani Kay
Nanga Inu bwanji
Verse 1
Usiku nitagona
Ninalotaa
thambo lamwamba
Litatsegukaa
mfumu yama fumu
Inatsika kumwamba
Kudzaweluzaa
Khamu LA anthu ochuluka linasonkhana
Kuzalandira fumu yawo
Yamtendele
Ndi khamu ya anjelo
Yoimba malipenga
Ndi azeze. Ndiyesu mwini
Anali nawo patsogolo
Atanyamula buku lake
Lamayina kulongosola zomwe iye anaziwona
Dziko lino
Anthu ochimwa adafuna
Atazemba nalowelera
mugulu lawolungama
Koma sizinatheke yesu anawadziwa
Nawafusa
Chorus
Nanga inu bwanji
Munkazuza ntundu wanuu
Nanga inu bwanji inu
Munadya chuma chasiye
Unali oipa iwe opondeleza osauka
Unali m'busa iwe osocheletsa nkhosa zanga
Verse 2
Usiku wanga kumaloto ndinawona
Mwala imene amisili anaukana
Zowona ndiwomwewo omwe unasanduka wapangodya
Yesu yemwe anthu ena anamunyoza
Namupachika kwapilatoo
Ndinawona ndinawona
Yemweyo
Anali oweluza dziko lino
Mpando wake wachifumu onyezima
Chakumanja kwa dzanja latate ake
Ndithudi ndiyemweyi yo yemweyo azaweluze dziko losee
Anthu ochimwa adzafuna atazembaa
Nalowelera mugulu lawolungamaa
Koma sizizatheka yesu azawadziwa nawafusaa
Chorus
Nanga inu bwa
Munkazuza NTundu wanuu
Nanga Inu bwanji
Munadya chuma chamasiyee
Unali oipa iwe
Opondeleza osaukaa
Unali m'busa iwe
Osocheletsa nkhosa zangaa