Letra da música
Ndi mitima yokondwera
Mbuye wathu tiyamika.
E, chifundo chake chonse
Ndichosatha nthawi zonse.
2 Dzina lake tibukitsa,
Mlungu ndiye yekhayekha.
3 Mphamvu yake inalenga
Dziko lonse ndikumwamba
4 Anatsogolera kale
M'chipululu anthu ake.
Ine dzakwera mwamba ndi angero ine ine. dzakwera mwambaaa ine dzakwera mwamba. ndi angero ine dzakwera mwambaaa ine. dzakwera mwambaaa. ndi angero ine dzakwera. mwambaaa.
5 Ndi chifundo atipenya
Ife anthu osauka.
6 Amaweta nyama zonse,
Zingasowe kanthu konse.
7 Tiimbire Mlungu wathu
Waulemu ndi wamkulu
8 Tithawire kwa Mulungu,
Ndiko tikapeze moyo.
Ine dzakwera mwamba ndi angero ine ine. dzakwera mwambaaa ine dzakwera mwamba. ndi angero ine dzakwera mwambaaa ine. dzakwera mwambaaa. ndi angero ine dzakwera. mwambaaa.